Jeremiah 6:16 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mau a Chauta ndi aŵa, “Imani pa mphambano, ndipo mupenye. Mufunse kumene kuli njira zakale ndi kumene kuli njira yabwino. Tsono mutsate njira yabwinoyo, ndipo mudzakhala pa mtendere. Koma inuyo mudati, ‘Sitidzaitsata.’
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Yehova atero, Imani m'njira ndi kuona, funsani za mayendedwe akale, m'menemo muli njira yabwino, muyende m'menemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu; koma anati, Sitidzayendamo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Yehova atero, Imani m'njira ndi kuona, funsani za mayendedwe akale, m'menemo muli njira yabwino, muyende m'menemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu; koma anati, Sitidzayendamo.