Job 34:37 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pa tchimo lao aonjezerapo upandu, akunyadira zochita zao, ndipo akuchulukitsa mau onyoza Mulungu ife tilikumva.” Mulungu amasamalira zochitika pa dziko lapansi.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti pa kuchimwa kwake aonjeza kupikisana ndi Mulungu, asansa manja pakati pa ife, nachulukitsa maneno ake pa Mulungu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti pa kucimwa kwace aonjeza kupikisana ndi Mulungu, Asansa manja pakati pa ife, Nacurukitsa maneno ace pa Mulungu.