John 1:47 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene Yesu adaona Natanaele akubwera potero, adati, “Mwamuwonatu Mwisraele weniweni wopanda chinyengo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Yesu anaona Natanaele alinkudza kwa Iye, nanena za iye, Onani, Mwisraele ndithu, mwa iye mulibe chinyengo!
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Yesu anaona Natanayeli alinkudza kwa iye, nanena za iye, Onani, M-israyeli ndithu, mwa iye mulibe cinyengo!