John 11:54 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Nchifukwa chake Yesu sankayenda poyera pakati pa anthu. Koma adachokako napita ku dziko limene linali pafupi ndi chipululu, ku mudzi wina dzina lake Efuremu, ndipo adakhala kumeneko pamodzi ndi ophunzira ake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chifukwa chake Yesu sanayandeyendanso poonekera mwa Ayuda, koma anachokapo kunka kudziko loyandikira chipululu, kumudzi dzina lake Efuremu; nakhala komweko pamodzi ndi ophunzira ake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Cifukwa cace Yesu sanayandeyendanso poonekera mwa Ayuda, koma anacokapo kunka ku dziko loyandikira cipululu, kumudzi dzina lace Efraimu; nakhala komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.