John 11:56 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ankamufunafuna Yesu, ndipo pamene adasonkhana m'Nyumba ya Mulungu ankafunsana kuti, “Kodi inu mukuganiza bwanji? Kodi monga Iye uja abwera kuchikondwerero kuno?”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo analikumfuna Yesu, nanena wina ndi mnzake poimirira iwo m'Kachisi, Muyesa bwanji inu, sadzadza kuchikondwerero kodi?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo analikumfuna Yesu, nanena wina ndi mnzace poimirira iwo m'Kacisi, Muyesa bwanji inu, sadzadza kuphwando kodi?