John 11:57 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anali atalamula kuti aliyense akadziŵa kumene kuli Yesu, aŵadziŵitse, kuti akamgwire.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma ansembe aakulu ndi Afarisi adalamula kuti, munthu wina akadziwa pokhala Iye, aulule, kuti akamgwire Iye.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma ansembe akulu ndi Afarisi adalamulira, kuti, munthu wina akadziwa pokhala iye, aulule, kuti akamgwire iye.