John 13:1 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Chikondwerero cha Paska chili pafupi, Yesu adaadziŵiratu kuti nthaŵi yake yafika yakuti achoke pansi pano kupita kwa Atate. Iye ankaŵakonda amene anali ake pansi pano, ndipo adaaŵakonda kotheratu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma pasanafike chikondwerero la Paska, Yesu, podziwa kuti nthawi yake idadza yakuchoka kutuluka m'dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m'mene anakonda ake a Iye yekha a m'dziko lapansi, anawakonda kufikira chimaliziro.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma pasanafike phwando la Paskha, Yesu, podziwa kuti nthawi yace idadza yakucoka kuturuka m'dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m'mene anakonda ace a iye yekha a m'dziko lapansi, anawakomia kufikira cimariziro.