John 13:29 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Popeza kuti Yudasi ankasunga thumba la ndalama, anzake ankayesa kuti Yesu akumuuza kuti, “Kagule zofunika paphwando pano,” kapena kuti akapereke kanthu kwa osauka.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pakuti popeza Yudasi anali nalo thumba, ena analikuyesa kuti Yesu ananena kwa iye, Gula zimene zitisowa pachikondwerero; kapena, kuti apatse kanthu kwa aumphawi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pakuti popeza Yudase anali nalo thumba, enaanalikuyesakuti Yesu ananena kwa iye, Gula zimene zitisowa paphwando; kapena, kuti apatse kanthu kwa aumphawi.