John 13:36 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Simoni Petro adafunsa Yesu kuti, “Ambuye, mukupita kuti?” Yesu adati, “Kumene ndikupita, sungathe kunditsatira tsopano ai, koma udzanditsatira bwino lino.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Simoni Petro anena ndi Iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, udzanditsata bwino lomwe.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Simoni Petro anena ndi iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, 2 udzanditsata bwino lomwe.