John 13:38 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Apo Yesu adati, “Iweyo kutaya moyo wako chifukwa cha Ine! Ndithu ndikunenetsa kuti tambala asanalire, ukhala utandikana katatu kuti Ine sundidziŵa.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Yesu anayankha, Moyo wako kodi udzautaya chifukwa cha Ine? Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Asanalire tambala udzandikana Ine katatu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Yesu anayankha, Moyo wako kodi udzautaya cifukwa ca Ine? Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Asanalire tambala udzandikana Ine katatu.