John 18:15 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Simoni Petro ndi wophunzira wina adatsatira Yesu. Wophunzira winayo anali wodziŵika kwa mkulu wa ansembe onse. Tsono iye adaloŵa pamodzi ndi Yesu m'bwalo la nyumba ya mkulu wa ansembeyo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Simoni Petro ndi wophunzira wina anatsata Yesu. Koma wophunzira ameneyo anali wodziwika kwa mkulu wa ansembe, nalowa pamodzi ndi Yesu, m'bwalo la mkulu wa ansembe;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Simoni Petro ndi wophunzira wina anatsata Yesu. Koma wophunzira ameneyo anali wodziwika kwa mkulu wa ansembe, nalowa pamodzi ndi Yesu, m'bwalo la mkulu wa ansembe;