John 18:2 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yudasi yemwe, amene adapereka Yesu kwa adani ake, ankaŵadziŵa malowo, pakuti Yesu ankapita kumeneko kaŵirikaŵiri ndi ophunzira ake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma Yudasinso amene akampereka Iye, anadziwa malowa; chifukwa Yesu akamkako kawirikawiri ndi ophunzira ake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma Yudasenso amene akampereka iye, anadziwa malowa; cifukwa Yesu akamkako kawiri kawiri ndi akuphunzira ace.