John 21:20 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Petro adacheuka, naona wophunzira uja amene Yesu ankamukonda kwambiri akuŵatsatira. Ndiye wophunzira yemwe uja amene adaatsamira pa chifukwa cha Yesu paphwando paja namufunsa kuti, “Ambuye, amene adzakuperekani kwa adani anu ndani?”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Petro, m'mene anacheuka, anapenya wophunzira amene Yesu anamkonda alikutsata, amenenso anatsamira pachifuwa pake pamgonero, nati, Ambuye, ndani iye wakupereka Inu?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Petro, m'mene anaceuka, anapenya wophunzira amene Yesu anamkonda alikutsata, amenenso anatsamira pacifuwa pace pamgonero, nati, Ambuye, ndani iye wakupereka Inu?