John 4:10 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yesu adati, “Mukadadziŵa mphatso ya Mulungu, mukadadziŵanso amene akupempha madzi akumwayu, bwenzi mutampempha ndi inuyo mai, Iye nakupatsani madzi opatsa moyo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha Iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.