John 4:42 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mwakuti adauza mai uja kuti, “Takhulupirira tsopano, osati chifukwa cha mau ako, koma chifukwa tadzimvera tokha. Tadziŵa kuti ameneyu ndi Mpulumutsidi wa anthu a pa dziko lonse lapansi.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
ndipo ananena kwa mkazi, kuti, Tsopano sitikhulupirira chifukwa cha kulankhula kwako: pakuti tamva tokha, ndipo tidziwa kuti Mpulumutsi wa dziko lapansi ndi Iyeyu ndithu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
ndipo ananena kwa mkazi, kuti, Tsopano sitikhulupira cifukwa ca kulankhula kwako: pakuti tamva tokha, ndipo tidziwa kuti Mpulumutsi wa dziko lapansi ndi Iyeyu ndithu.