John 8:28 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Yesu adaŵauza kuti, “Mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziŵa kuti Ine ndine Ndilipo. Mudzadziŵanso kuti sindichita kanthu pandekha, ndimalankhula zimene Atate adandiphunzitsa.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Chifukwa chake Yesu anati, Pamene mutadzamkweza Mwana wa Munthu, pomwepo mudzazindikira kuti Ine ndine, ndipo sindichita kanthu kwa Ine ndekha, koma monga anandiphunzitsa Atate, ndilankhula izi.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Cifukwa cace Yesu anati, Pamene mutadzamkweza Mwana wa munthu, pomwepo mudzazindikira kuti Ine ndine, ndipo sindicita kanthu kwa Ine ndekha, koma monga anandiphunzitsa Atate, ndilankhula izi.