Joshua 16:6 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kuchokera kumeneko malirewo adatsikira mpaka ku nyanja. Mikimetati anali kumpoto kwake. Kuvuma malirewo adakhotera cha ku Taanatisilo, napitirira malo amenewo chakuvuma, mpaka kukafika ku Yanowa.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
natuluka malire kumadzulo ku Mikametati kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kunka ku Taanatisilo, naupitirira kum'mawa kwake kwa Yanowa:
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Malirewo anapitirira mpaka ku nyanja. Mikimetati anali kumpoto kwake. Kuchokera kumeneko anakhotera cha kummawa kuloza ku Taanati Silo ndi kudutsa kumeneko cha kummawa mpaka ku Yanowa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
naturuka malire kumadzulo ku Mikametatu kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kumka ku Taanatu-silo, naupitirira kum'mawa kwace kwa Yanoa: