Joshua 18:8 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono anthuwo adapitadi kukalemba za dzikolo, Yoswa ataŵalangiza kuti, “Pitani, kaliyendereni dziko lonselo, ndipo mukalembe bwino za dzikolo. Tsono mutatero, mubwererenso kwa ine kuno. Ine ndidzakuchitirani maere pamaso pa Chauta konkuno ku Silo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo amunawo ananyamuka, namuka; ndipo Yoswa analamulira opita kulemba dzikowo, ndi kuti, Mukani, muyendeyende pakati pa dziko, ndi kulilemba, nimubwerenso kwa ine, ndipo ndidzakuloterani maere pano pamaso pa Yehova pa Silo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo amunawo ananyamuka, namuka; ndipo Yoswa analamulira opita kulemba dzikowo, ndi kuti, Mukani, muyendeyende pakati pa dziko, ndi kulilemba, oimubwerenso kwa ine, ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova pa Silo.