Judges 2:19 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma nthaŵi zonse mtsogoleri akafa, anthuwo ankayambanso kuchita zoipa, nkusanduka oipa kupambana makolo ao, namatsata milungu ina, kumaitumikira ndi kumaigwadira. Sankaleka kuchita zimene adaazoloŵera ndiponso sankaleka kukhala ouma mitu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma kunali atafa woweruzayo anabwerera m'mbuyo, naposa makolo ao ndi kuchita moipitsa, ndi kutsata milungu ina kuitumikira ndi kuigwadira, sanaleke kanthu ka machitidwe ao kapena ka njira yao yatcheni.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma kunali atafa woweruzayo anabwerera m'mbuyo, naposa makolo ao ndi kucita moipitsa, ndi kutsata milungu yina kuitumikira ndi kuigwadira, sanaleka kanthu ka macitidwe ao kapena ka njira yao yacheni.