Judges 6:27 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Choncho Gideoni adatenga anthu khumi mwa atumiki ake, ndipo adachitadi monga momwe Chauta adaamuuzira. Koma popeza kuti ankaopa kwambiri a m'banja la bambo wake ndiponso anthu am'mudzimo, sadachite zimenezo masana, adachita usiku.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo Gideoni anatenga amuna khumi mwa anyamata ake, nachita monga Yehova adanena naye; ndipo kunali, popeza anaopa akunyumba ya atate wake, ndi amuna akumudziwo, sanachichite msana, koma usiku.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo Gideoni anatenga amuna khumi mwa anyamata ace, nacita monga Yehova adanena naye; ndipo kunali, popeza anaopa a ku nyumba ya atate wace, ndi amuna a ku mudziwo, sanacicita msana, koma usiku.