Leviticus 14:49 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mwiniwake wa nyumbayo atenge timbalame tiŵiri, nthambi yamkungudza, kansalu kamlangali, ndi kachitsamba ka hisope, kuti zikhale zoyeretsera nyumbayo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo atenge mbalame ziwiri, ndi mtengo wamkungudza, ndi ubweya wofiira, ndi hisope, kuti ayeretse nazo nyumbayo;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo atenge mbalame ziwiri, ndi mtengo wamkungudza, ndi ubweya wofiira, ndi hisope, kuti ayeretse nazo nyumbayo;