Leviticus 3:13 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo, ndipo aiphere pakhomo pa chihema chamsonkhano. Pambuyo pake ana a Aroni aliwaze magazi guwa molizungulira.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
naike dzanja lake pamutu pake, naiphe pa khomo la chihema chokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wake pa guwa la nsembe pozungulira.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
naike dzanja lace pamutu pace, naiphe pa khomo la cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.