Leviticus 4:35 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono achotse mafuta ake onse, monga momwe amachotsera mafuta a nkhosa yoperekera nsembe yachiyanjano. Ndipo aŵatenthe pa guwa, pamodzi ndi nsembe zina zopsereza pa moto, zopereka kwa Chauta. Umu ndimo m'mene wansembe azichitira mwambo wopepesera tchimo la munthu, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
nawachotse mafuta ake onse, monga umo amachotsera mafuta a nkhosa pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo atenthe awa pa guwa la nsembe, monga umo amachitira nsembe zamoto za Yehova; ndipo wansembeyo amchitire chomtetezera pa kuchimwa kwake adakuchimwira, ndipo adzakhululukidwa.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
nawacotse mafuta ace onse, monga umo amacotsera mafuta a nkhosa pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo atenthe, awa pa guwa la nsembe, monga umo amacitira nsembe zamoto za Yehova; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera pa kucimwa kwace adakucimwira, ndipo adzakhululukidwa.