Leviticus 7:14 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kenaka atengeko mtanda umodzi pa mtundu uliwonse wa buledi, kuti ukhale nsembe yopereka kwa Chauta. Mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe zachiyanjano.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo pa zopereka zonsezi atengepo ndi kubwera nako kamtanda kamodzi, kuti kakhale ka nsembe yokweza ya kwa Yehova; kakhale ka wansembe wakuwaza mwazi wa nsembe zoyamika.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo pa zopereka zonsezi atengepo ndi kubwera nako kamtanda kamodzi, kuti kakhale ka nsembe yokweza ya kwa Yehova; kakhale ka wansembe wakuwaza mwazi wa nsembe zoyamika.