Leviticus 8:29 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ndipo adatenga nganga naiweyula kuti ikhale chopereka choweyula pamaso pa Chauta. Chimenecho ndicho chigawo cha Mose cha nkhosa yamphongo yopereka pa mwambo wodzoza ansembe, potsata malamulo a Chauta kwa Mose.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Mose anatenga ngangayo naiweyula, nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndilo gawo la Mose la ku nkhosa yamphongo ya kudzaza manja; monga Yehova adamuuza Mose.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Mose anatenga ngangayo naiweyula, nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndilo gawo la Mose la ku nkhosa yamphongo ya kudzaza manja; monga Yehova adamuuza Mose.