Luke 7:6 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono Yesu adapita nawo. Pamene Iye ankayandikira nyumba yake, mkulu wa asilikali uja adatuma abwenzi ake kwa Yesu kukamuuza kuti, “Ambuye, musadzivute, pakuti sindili woyenera kuti Inu nkuloŵa m'nyumba mwanga.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika Iye tsono pafupi panyumba yake, kenturiyo anatuma kwa Iye abwenzi ake, kunena naye, Ambuye, musadzivute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa chindwi langa;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Pamenepo Yesu anapita nawo. Iye sanali patali ndi nyumba pamene Kenturiyo anatumiza anzake kuti akamuwuze kuti, “Ambuye, musadzivutitse, pakuti ndine wosayenera kuti mulowe mʼnyumba mwanga.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika iye tsono pafupi panyumba yace, kenturiyo anatuma kwa iye abwenzi ace, kunena naye, Ambuye, musadzibvute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa chindwi langa;