Mark 10:32 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene iwo anali pa ulendo wopita ku Yerusalemu, Yesu ankayenda patsogolo pa ophunzira ake. Ophunzirawo anali oda nkhaŵa kwambiri. Ndipo anthu amene ankaŵatsatira anali ndi mantha. Yesu adaŵaitaniranso pambali ophunzira khumi ndi aŵiri aja, nayamba kuŵafotokozera zimene zinalikudzamugwera.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo iwo anali m'njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anachita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ali pa ulendo wawo wopita ku Yerusalemu, Yesu ali patsogolo, ophunzira ake anadabwa, ndipo amene amamutsatira amachita mantha. Anatenganso ophunzira ake khumi ndi awiri pa mbali ndipo anawawuza zimene zikamuchitikire Iye.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo iwo anali m'njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anacita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,