Mark 8:27 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yesu ndi ophunzira ake adapita ku midzi ya ku Kesareya-Filipi. Pa njira Yesu adafunsa ophunzira akewo kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo anatuluka Yesu, ndi ophunzira ake, nalowa kumidzi ya ku Kesareya-Filipi; ndipo panjira anafunsa ophunzira ake, nanena nao, Kodi anthu ananena kuti Ine ndine yani?
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo anaturuka Yesu, ndi ophunzira ace, nalowa ku midzi ya ku Kaisareya wa Filipi; ndipo panjira anafunsa ophunzira ace, nanena nao, Kodi anthu anena kuti Ine ndine yani?