Matthew 1:23 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Namwali wina wosadziŵa mwamuna adzatenga pathupi nkubala mwana wamwamuna. Mwanayo adzatchedwa dzina loti Imanuele,” ndiye kuti “Mulungu ali nafe.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, ndipo adzamutcha dzina lake, Imanuele. Ndilo losandulika, Mulungu nafe.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Onani namwali adzaima, Nadzabala mwana wamwamuna, Ndipo adzamucha dzina lace, Emanueli; ndilo losandulika, Mulungu nafe.