Matthew 16:21 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Kuyambira nthaŵi imeneyo Yesu adayamba kudziŵitsa ophunzira ake kuti, “Ndiyenera kupita ku Yerusalemu, kumeneko akulu a Ayuda ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi a Malamulo adzandizunza kwambiri. Ndidzaphedwa koma mkucha wake ndidzauka.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kuwalangiza ophunzira ake, kuti kuyenera Iye amuke ku Yerusalemu, kukazunzidwa zambiri ndi akulu, ndi ansembe aakulu, ndi alembi; ndi kukaphedwa, ndi tsiku lachitatu kuuka kwa akufa.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Kuyambira nthawi imeneyo Yesu anayamba kuwafotokozera ophunzira ake kuti Iye ayenera kupita ku Yerusalemu ndi kukazunzidwa kwambiri mʼmanja mwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo kuti ayenera kuphedwa, ndi kuti tsiku lachitatu adzaukitsidwa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kuwalangiza ophunzira ace, kuti kuyenera Iye amuke ku Yerusalemu, kukazunzidwa zambiri ndi akuru, ndi ansembe akuru, ndi alembi; ndi kukaphedwa, ndi tsiku lacitatu kuuka kwa akufa.