Matthew 21:12 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Yesu adaloŵa m'Nyumba ya Mulungu, nayamba kutulutsa onse amene ankachita malonda m'menemo. Adagubudula matebulo a osinthitsa ndalama, ndiponso mipando ya ogulitsa nkhunda.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yesu analowa ku Kachisi wa Mulungu natulutsira kunja onse akugulitsa ndi kugula malonda, nagubuduza magome a osintha ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yesu analowa mʼdera lina la Nyumba ya Mulungu ndipo anatulutsa kunja anthu onse amene ankachita malonda. Anagubuduza matebulo a osinthira ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yesu analowa ku Kacisi wa Mulungu naturutsira kunja onse akugulitsa ndi kugula malonda, nagubuduza magome a osintha ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;