Matthew 8:18 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Pamene Yesu adaona chinamtindi cha anthu amene adaamuzinga, adauza ophunzira ake kuti, “Tiyeni tiwolokere tsidya linalo.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke kutsidya lina.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke ku tsidya lina,