Matthew 9:10 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Tsono pamene Yesu ankadya m'nyumba, kudabwera anthu ambiri okhometsa msonkho, ndi anthu ochimwa, kudzadya nao ndi Yesuyo ndi ophunzira ake.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo panali pamene Iye analinkukhala pachakudya m'nyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anadza nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo panali pamene Iye analinkukhala pacakudya m'nyumba, onani, amisonkho ndi ocimwa ambiri anadza nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ace.