Micah 7:4 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Munthu wabwino koposa ali ngati lunguzi, wolungama koposa ndi wolasa ngati tchinga laminga. Lafika tsiku la chilango, limene alonda ao, aneneri, adanena. Lafika tsiku la chisokonezo chao.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Wokoma wa iwo akunga mitungwi; woongoka wao aipa koposa mpanda waminga; tsiku la alonda ako la kulangidwa kwako lafika, tsopano kwafika kuthedwa nzeru kwao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Wokoma wa iwo akunga mitungwi; woongoka wao aipa koposa mpanda waminga; tsiku la alonda ako la kulangidwa kwako lafika, tsopano kwafika kuthedwa nzeru kwao.