Nahum 1:15 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ona, kumapiri kukubwera munthu, iyeyu ali ndi uthenga wabwino, akulengeza za mtendere. Inu a ku Yuda muzisunga masiku achikondwerero; zimene mudalumbira, muzizichitadi. Anthu oipawo sadzakuthiraninso nkhondo. Adaonongeka kotheratu.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Taonani pamapiri mapazi a iye wakulalikira uthenga wabwino, wakubukitsa mtendere! Chita chikondwerero chako, Yuda, kwaniritsa zowinda zako; pakuti wopanda pakeyo sadzapitanso mwa iwe; iye waonongeka konse.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Taonani pamapiri mapazi a iye wakulalikira uthenga wabwino, wakubukitsa mtendere! cita madyerero ako, Yuda, kwaniritsa zowinda zako; pakuti wopanda paceyo sadzapitanso mwa iwe; iye waonongeka konse.