Nehemiah 12:26 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Ameneŵa ndiwo adaalipo pa nthaŵi ya Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndiponso pa nthaŵi ya bwanamkubwa Nehemiya ndi wansembe Ezara amene analinso katswiri wa malamulo.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Awa anakhala m'masiku a Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndi m'masiku a Nehemiya kazembe, ndi a Ezara wansembe mlembiyo.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Iwo ndiwo ankatumikira pa nthawi ya Yowakimu mwana wa Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndiponso pa nthawi ya bwanamkubwa Nehemiya ndi wansembe Ezara amene analinso mlembi.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Awa anakhala m'masiku a Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndi m'masiku a Nehemiya kazembe, ndi a Ezara wansembe mlembiyo.