Nehemiah 8:17 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Motero onse amene adaasonkhana, ndiye kuti amene adaabwerako ku ukapolo, adamanga misasa, ndipo adakhala m'menemo. Kuyambira nthaŵi ya Yoswa, mwana wa Nuni, mpaka tsiku limenelo, Aisraele anali asanachitepo zoterozo. Motero kunali chikondwerero chachikulu kwambiri.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndi msonkhano wonse wa iwo otuluka m'ndende anamanga misasa, nakhala m'misasamo; pakuti chiyambire masiku a Yoswa mwana wa Nuni kufikira tsiku lija ana a Israele sanatero. Ndipo panali chimwemwe chachikulu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndi msonkhano wonse wa iwo oturuka m'ndende anamanga misasa, nakhala m'misasamo; pakuti ciyambire masiku a Yesuwa mwana wa Nuni kufikira tsiku lija ana a Israyeli sanatero. Ndipo panali cimwemwe cacikuru.