Nehemiah 9:3 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Anthuwo adaimirira pomwepo, ndipo adamva mau a m'buku la Malamulo a Chauta akuŵaŵerenga nthaŵi yokwanira maora atatu. Pa maora atatu enanso, anthuwo ankaulula machimo ao namapembedza Chauta, Mulungu wao.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Naimirira poima pao, nawerenga m'buku la chilamulo cha Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anawulula, napembedza Yehova Mulungu wao.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Anthuwo anayimirira pomwepo, ndipo anamva mawu a mʼbuku la malamulo a Yehova akuwerengedwa kwa maora enanso atatu ndipo anakhala maora ena atatu akuwulula machimo awo ndi kupembedza Yehova Mulungu wawo.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Naimima poima pao, nawerenga m'buku la cilamulo ca Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anaulula, napembedza Yehova Mulungu wao.