Nehemiah 9:30 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mudaŵapirira zaka zambiri ndipo munkaŵachenjeza ndi mzimu wanu kudzera mwa aneneri anu, komabe sadafune kutchera khutu. Nchifukwa chake mudaŵapereka kwa anthu a m'maiko ena.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Koma munawalekerera zaka zambiri, ndi kuwachitira umboni ndi mzimu wanu, mwa aneneri anu, koma sanamvere; chifukwa chake munawapereka m'dzanja la mitundu ya anthu a m'dziko.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Munapirira nawo kwa zaka zambiri. Munkawachenjeza ndi Mzimu wanu kudzera mwa aneneri anu, koma iwo sankakumverani. Choncho munawapereka mʼmanja mwa anthu a mayiko ena.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Koma munawalekerera zaka zambiri, ndi kuwacitira umboni ndi mzimu wanu, mwa aneneri anu, koma sanamvera; cifukwa cace munawapereka m'dzanja la mitundu ya anthu a m'dziko.