Numbers 16:37 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Uza Eleazara, mwana wa wansembe Aroni, kuti achotse zofukizira lubani zija m'motomo, ndipo motowo aumwazire kutali.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Nena ndi Eleazara mwana wa Aroni wansembe, kuti aphule mbale zofukiza pakati pa moto, nutaye makalawo uko kutali: pakuti zili zopatulika;
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Nena ndi Eleazara mwana wa Aroni wansembe, kuti aphule mbale zofukiza pakati pa moto, nutaye makalawo uko kutali; pakuti ziri zopatulika;