Numbers 16:38 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Zofukizira za anthu amene aphedwa chifukwa cha kuchimwa kwao nzoyera. Zofukizirazo azisule chophimbira pa guwa, poti azipereka pamaso pa Chauta, nchifukwa chake nzoyera. Motero zidzakhala chizindikiro kwa Aisraele onse.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
mbale zofukizazo za iwo amene adachimwira moyo waowao, ndipo azisule zaphanthiphanthi, zikhale chivundikiro cha guwa la nsembe; popeza anabwera nazo pamaso pa Yehova, chifukwa chake zikhala zopatulika; ndipo zidzakhala chizindikiro kwa ana a Israele.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
mbale zofukizazo za iwo amene adacimwira moyo wao wao, ndipo azisule zaphanthiphanthi, zikhale cibvundikilo ca guwa la nsembe; popeza anabwera nazo pamaso pa Yehova, cifukwa cace zikhala zopatulika; ndipo zidzakhala cizindikilo kwa ana a Israyeli.