Numbers 20:12 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Chauta adauza Mose ndi Aroni kuti, “Popeza kuti simudandikhulupirire, ndipo simudasonyeze pamaso pa Aisraele kuti ndine woyera, simudzaŵaloŵetsa anthuŵa m'dziko limene ndaŵapatsa.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Popeza simunandikhulupirira Ine, kundipatula Ine pamaso pa ana a Israele, chifukwa chake simudzalowetsa msonkhano uwu m'dziko ndinawapatsali.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Popeza simunandikhulupirira Ine, kundipatula Ine pamaso pa ana a Israyeli, cifukwa cace simudzalowetsa msonkhano uwu m'dziko ndinawapatsali.