Numbers 21:34 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Koma Chauta adauza Mose kuti, “Usamuwope. Ndampereka m'manja mwako pamodzi ndi anthu ake onse ndi dziko lake lomwe. Ndipo umchite zomwe udachita Sihoni mfumu ya Aamori amene ankakhala ku Hesiboni.”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo Yehova anati kwa Mose, Usamuopa; popeza ndampereka m'manja mwako, iye ndi anthu ake onse, ndi dziko lake; umchitire monga umo unachitira Sihoni mfumu ya Aamori anakhalayo ku Hesiboni.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo Yehova anati kwa Mose, Usamuopa; popeza ndampereka m'manja mwako, iye ndi anthu ace onse, ndi dziko lace; umcitire monga umo unacitira Sihoni mfumu ya Aamori anakhalayo ku Hesiboni.