Philippians 1:26 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Motero pamene ndidzafikanso kwanuko, mudzakhala ndi zifukwa zochuluka zonyadira Khristu Yesu chifukwa cha ine.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
kuti kudzitamandira kwanu kuchuluke m'Khristu Yesu mwa ine, mwa kukhalanso ine kwa inu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
kuti kudzitamandira kwanu kucuruke m'Kristu Yesu mwa ine, mwa kukhalanso ine kwa inu.