Psalms 31:15 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Masiku anga ali m'manja mwanu. Pulumutseni kwa adani anga ndi kwa ondizunza.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Nyengo zanga zili m'manja mwanu, mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Nyengo zanga ziri m'manja mwanu: Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.