Revelation 11:13 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Nthaŵi yomweyo kudachita chivomezi chachikulu, mwakuti chimodzi mwa zigawo khumi za mzinda chidagwa, ndipo anthu zikwi zisanu ndi ziŵiri adaphedwa ndi chivomezicho. Otsalawo adaopsedwa kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wa Kumwamba.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ndipo panthawipo panali chivomezi chachikulu, ndipo limodzi la magawo khumi a mudzi lidagwa; ndipo anaphedwa m'chivomezicho anthu zikwi zisanu ndi ziwiri; ndipo otsalawo anakhala amantha, napatsa ulemerero kwa Mulungu wa m'Mwamba.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ndipo panthawipo panali cibvomezi cacikuru, ndipo limodzi la magawo khumi a mudzi Iidagwa; ndipo anaphedwa m'cibvomezico anthu zikwi zisanu ndi ziwiri; ndipo otsalawo anakhala amantha, napatsa ulemerero kwa Mulungu wa m'Mwamba.