Revelation 11:6 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mbonizo zili ndi mphamvu zomanga mvula kuti isagwe masiku amene iwo akulalika mau ochokera kwa Mulungu. Zili ndi mphamvu zosandutsira madzi kuti akhale magazi. Ndipo zili ndi mphamvu zodzetsera mliri uliwonse pa dziko lapansi, nthaŵi iliyonse imene zingafune.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Izo zili nao ulamuliro wakutseka m'mwamba, isagwe mvula masiku a chinenero chao; ndipo ulamuliro zili nao pamadzi kuwasandutsa mwazi, ndi kupanda dziko ndi mliri uliwonse nthawi iliyonse zikafuna.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Izo ziti nao ulamuliro wakutseka m'mwamba, isagwe mvula masiku a cinenero cao; ndipo ulamuliro ziti nao pamadzi kuwasandutsa mwazi, ndi kupanda dziko ndi mliri uli wonse nthawi iri yonse zikafuna.