Revelation 22:16 — Compare Translations

4 translations compared side by side

Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
“Ine, Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti akufotokozereni zimenezi ndipo zithandize mipingo. Ine ndine chiphukira chotuluka mwa mfumu Davide, ndine chidzukulu chake. Ndine Nthanda, nyenyezi yoŵala m'mamaŵa!”
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Ine Yesu ndatuma mngelo wanga kukuchitirani umboni za izi m'Mipingo. Ine ndine muzu ndi mbadwa ya Davide, nyenyezi yonyezimira ya nthanda.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Ine Yesu ndatuma mngelo wanga kukucitirani umboni za izi m'Mipingo. Ine ndine muzo ndi mbadwa ya Davide, nyenyezi yonyezimira ya nthanda.