Romans 3:27 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Iyai, sanganyade konse. Chifukwa chiyani? Chifukwa chakuti pamaso pa Mulungu chachikulu si ntchito zabwino zimene munthu amachita, koma chachikulu nkuti munthu azikhulupirira.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Pamenepo kudzitama kuli kuti? Kwaletsedwa. Ndi lamulo lotani? La ntchito kodi? Iai; koma ndi lamulo la chikhulupiriro.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Pamenepo kudzitama kuli kuti? Kwaletsedwa. Ndi lamulo lotani? La nchito kodi? lai; koma ndi lamulo la cikhulupiriro.