Zechariah 14:21 — Compare Translations
4 translations compared side by side
Chewa (Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa)
Mbiya iliyonse ya ku Yerusalemu ndi ku Yuda idzakhala yoperekedwa kwa Chauta Wamphamvuzonse. Onse opereka nsembe ku Yerusalemu adzagwiritsa ntchito mbiyazo pophika nyama za nsembe. Nthaŵi imeneyo ikadzafika, sipadzaonekanso wamalonda aliyense m'Nyumba ya Chauta Wamphamvuzonse.
Chewa 1922 (Buku Lopatulika)
Inde mbiya zonse za m'Yerusalemu ndi m'Yuda zidzakhala zopatulikira Yehova wa makamu; ndi onse akuphera nsembe adzafika nadzatengako, ndi kuphikamo; ndipo tsiku lomwelo simudzakhalanso Mkanani m'nyumba ya Yehova wa makamu.
Chewa 2002 (Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero)
Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Chewa Bible (BL) 1992 - Buku Lopatulika
Inde mbiya zonse za m'Yerusalemu ndi m'Yuda zidzakhala zopatulikira Yehova wa makamu; ndi onse akuphera nsembe adzafika nadzatengako, ndi kuphikamo; ndipo tsiku lomwelo simudzakhalanso Mkanani m'nyumba ya Yehova wa makamu.